1 Chronicles 8

Adzukulu a Benjamini ndi Sauli

1Benjamini anabereka Bela mwana wake woyamba,
wachiwiri Asibeli, wachitatu Ahara,
2wachinayi Noha ndipo wachisanu Rafa.
3Ana a Bela anali awa:
Adari, Gera, Abihudi,
4Abisuwa, Naamani, Ahowa, 5Gera, Sefufani ndi Hiramu.
6Zidzukulu za Ehudi, zimene zinali atsogoleri a mabanja a amene amakhala ku Geba ndipo zinasamutsidwa kupita ku Manahati zinali izi:
7Naamani, Ahiya ndi Gera, amene anawasamutsa ndipo anabereka Uza ndi Ahihudi.
8Saharaimu anabereka ana ku Mowabu atalekana ndi akazi ake, Husimu ndi Baara. 9Mwa mkazi wake Hodesi anabereka Yobabu, Zibiya, Mesa, Malikamu, 10Yeusi, Sakiya ndi Mirima. Awa ndiye ana ake, atsogoleri a mabanja awo. 11Mwa mkazi wake Husimu anabereka Abitubi ndi Elipaala.
12Ana a Elipaala anali awa:
Eberi, Misamu, Semedi (amene anamanga mizinda ya Ono ndi Lodi ndi midzi yake yozungulira)
13ndiponso Beriya ndi Sema, amene anali atsogoleri a mabanja a amene ankakhala ku Ayaloni ndipo anathamangitsa nzika za ku Gati.
14Ahiyo, Sasaki, Yeremoti, 15Zebadiya, Aradi, Ederi, 16Mikayeli, Isipa ndi Yoha anali ana a Beriya.
17Zebadiya, Mesulamu, Hiziki, Heberi, 18Isimerai, Iziliya ndi Yobabu anali ana a Elipaala.
19Yakimu, Zikiri, Zabidi, 20Elienai, Ziletai, Elieli, 21Adaya, Beraya ndi Simirati anali ana a Simei.
22Isipani, Eberi, Elieli, 23Abidoni, Zikiri, Hanani, 24Hananiya, Elamu, Anitotiya, 25Ifideya ndi Penueli anali ana a Sasaki.
26Samuserai, Sehariya, Ataliya, 27Yaaresiya, Eliya ndi Zikiri anali ana a Yerohamu.
28Onsewa anali atsogoleri a mabanja, anthu otchuka potsata mibado yawo, ndipo ankakhala mu Yerusalemu.

29Yeiyeli amene amabereka Gibiyoni ankakhala ku Gibiyoni.
Dzina la mkazi wake linali Maaka,
30ndipo mwana wake woyamba anali Abidoni, motsatana ndi Zuri, Kisi, Baala, Neri, Nadabu, 31Gedori, Ahiyo, Zekeri 32ndi Mikiloti, amene anabereka Simea. Iwowa ankakhalanso ku Yerusalemu ndi abale awo.
33Neri anabereka Kisi. Kisi anabereka Sauli, ndipo Sauli anabereka Yonatani, Maliki-Suwa, Abinadabu ndi Esibaala.
34Mwana wa Yonatani anali
Meri-Baala, amene anabereka Mika.
35Ana a Mika anali awa:
Pitoni, Meleki, Tareya ndi Ahazi.
36Ahazi anabereka Yehoyada, Yehoyada anabereka Alemeti, Azimaveti ndi Zimuri, ndipo Zimuri anabereka Moza. 37Moza anabereka Bineya. Ana ake anali Rafa, Eleasa ndi Azeli.
38Azeli anali ndi ana asanu ndi mmodzi, ndipo mayina awo anali awa:
Azirikamu, Bokeru, Ismaeli, Seariya, Obadiya ndi Hanani. Onsewa anali ana a Azeli.
39Ana a Eseki mʼbale wake anali awa:
Mwana wake woyamba Ulamu, wachiwiri Yeusi ndipo wachitatu Elifeleti.
40Ana a Ulamu anali asilikali olimba mtima amene amadziwa kugwiritsa ntchito uta. Iwo anali ndi ana ndi adzukulu ambiri ndipo onse analipo 150.
Onsewa anali adzukulu a Benjamini.
Copyright information for NyaCCL